Mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Fransisko wapempha kuti mgwirizano omwe ulipo pakati pa mpingowu ndi mpingo wa Orthodox upitilire kuyenda bwino.
Papa amalankhula izi la mulungu mdziko la Armenia pambuyo pa mwambo wa nsembe ya misa yomwe anachitira limodzi ndi mpingo wa Orthodox pa ulendo wake wa masiku atatu wokacheza mdzikolo.
Papa anayamikira mtsogoleri wa mpingo wa Orthodox mdzikolo a Catholicos Karekin kamba ka chikondi chomwe wamuwonetsera pa ulendo wake wokayendera dzikolo.
Malipoti a wailesi ya Vatican ati Papa anali okondwa kamba koti apemphelera limodzi, agawana mphatso komanso mfundo zofuna kupititsa patsogolo mipingoyi.