Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mpingo Wa Anglican Wadzodza Ansembe Atatu

$
0
0

Mpingo wa Anglican mu dayosizi ya Upper Shire loweruka wadzoza madikoni atatu kukhala ansembe.

Polankhula pa mwambowu Episkopi wa dayosiziyi Ambuye Brighton Vita Malasa ayamikira ansembe atsopanowa podzipereka kutumikira Mulungu kudzera mu njira ya unsembe.

Iwo ati pozindikira kuti ansembe akusowa, apempha atumiki atsopanowa kuti akalimbikire pa utumiki wao kulikonse komwe atumidwe kukatumikira.

“Lero ndi tsiku lalikulu muno mu dayosizi ya Uppershire lomwe timadzodza ansembe atatu atsopano omwe akatumikire ma parishi osiyanasiyana kugwira ncthito ya Mulungu chifukwa ndi Iye amene waatuma. Tikuthokoza Mulungu kuti anyamata amenewa adzipereka komanso kuti watipatsa ife mphatso ya atumiki amenewa chifukwa masiku ano ansembe akuchepa ndipo akusowa,” anatero Ambuye Malasa.

Poyankhulapo yemwe anali mlendo wolemekezeka patsikuli yemwe ndi nduna ya zofalitsa nkhani ndikuphunzitsa anthu, Mayi Patricia Kaliati MP, ati mpingo wa Anglican umathandizana ndi boma potumikira anthu ake choncho anapempha mpingowu kuti upitirize kuthandiza boma pa ntchito za chitukuko mdziko muno.

“Boma limagwira ntchito ndi mpingo wa Anglican komanso mipingo yonse imene ili mdziko muno choncho tawona chofunikira kuti tichite nawo mwambowu ngati njira imodzi yowathokozera pa zinthu zomwe amatichitira monga kumanga zipatala, sukulu ndi zitukuko zina. Tikuwapempha kuti apitirize ulaliki wawo pa dziko lonse lapansi kuti pakutha pa moyo uno tikalandire kolona,” anatero Mayi Kaliati.

A Kaliati anati, “Ansembe atsopanowa tawapempha kuti apite akalalike monga anachitira ambuye athu Yesu Khristu komanso akamange mabanja ndikupereka ulangizi waukulu kuti akhale mabanja amene Mulungu akakondwere nawo.”


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>