Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Ayikiza M’mapemphero Anthui Okhuzidwa ndi Chiwembu Mdziko la Turkey

$
0
0

Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Fransisko anapempha mphindi yokhala chete pofuna kuyikiza mmapemphero anthu onse omwe akhudzidwa ndi chiwembu chomwe chachitika  pa bwalo lina la ndege mu mzinda  wa Istanbul mdziko la Turkey.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya Vatican Papa anachita izi lero ndi alendo omwe amakayendera likulu la mpingowu omwe amasonkhana nawo lachitatu lililonse.

Papa anati awayikiza mmapemphero anthu onse omwe akhudzidwa pa chiwembuchi ngakhalenso mabanja awo.

Malipoti ati padakali pano chiwerengero cha anthu omwe afa powomberedwa ngakhalenso ndi mabomba omwe anaphulitsidwa pa chiwembuchi ndi chokwana 41 ndipo ena   239 avulala ndipo ati gulu la zauchifwamba la Islamic State ndi lomwe lachita chiwembuchi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>