Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Radio Maria Malawi Yapempha Anthu Akwaniritse Malonjezo awo a Mariatona

$
0
0

Abwenzi a Radio Maria Malawi komanso anthu akufuna kwabwino awapempha kuti akwaniritse lonjezo lawo lothandiza wailesiyi pamene Mariatona wa chaka chino akupita kumapeto.

Wapampando wa Mariatona ya chaka chino a Emmanuel Kaliati anena izi pomwe Mtolankhani wathu amafuna kudziwa za momwe wailesiyi yakonzera dongosolo la mwambo wotsekera mariatonayi omwe uchitikire ku phiri la Michiru ku Chilomoni mu Ark-dayosizi ya Blantyre.

“Pa 2 July tili ku Michiru kukatsekera ulendo womwe tinauyamba pa 7 May ku Balaka. Mwambo ukayamba 6 koloko m’mawa ndi kukwera phiri popemphera kolona. Tikatsekera sikuti zonse zathera pompa ayi. Inu amene muli nako mwina mumadikira mwezi kuti uthe mutha kutumiza kangachepeko ndipo tikukumemezani nonse amene munapanga pledge kuti chonde kwaniritsani malonjezo anu kuti zonse ziyende bwino,” anatero a Kaliati.

Pa Mariatona wa chaka chino, Radio Maria Malawi ikufuna 10 million kwacha kuti imange goloto la Amai Maria, kugula chipangizo cha magetsi cha UPS komanso kubweza ngongole ku bungwe loyang’anira nyumba zoulutsa mawu mdziko muno la MACRA.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles