Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mphunzitsi Amangidwa Kamba Kogwilirira Mwana wa Sukulu

$
0
0

Apolisi m’boma la Ntchisi amanga mphunzitsi wa pa sukulu ina ya pulayimale kamba kogwirira ophunzira wina pa sukulupo wa zaka 16 zakubadwa.

Mneneri wa apolisi m’bomalo Sergent  Gladson M’bumpha watsimikizira Radio Maria Malawi za nkhaniyi ndipo wati Mphunzitsiyo, Justice Zambira wa zaka 24 zakubadwa anagwililira mtsikanayu kanayi pa sukulu ya pulayimale ya Kayoyo.

Sergent M’bumpha wati mphunzitsiyo wakhala akuyitana mtsikanayu kunyumba kwake kuti azikamugwilira ntchito za pakhomo ndipo akamaliza ati ndi pomwe amamugwililira. Mtsikanayu ati anakauza makolo ake za nkhaniyi omwe anakanena ku polisi ndipo malipoti a ku chipatala chaching’ono cha Nthondo atsimikiza za mchitidwewu.

Mphunzitsiyu atafunsidwa ndi apolisi ati anavomera za nkhaniyi ndipo kuti iye amachita izi kamba koti mtsikanayo anamuuza kuti ali ndi zaka zoposera 18.

A Justice Zambira akuyembekezeka kukawonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe  mlandu wogwiririra ndipo iwo amachokera mmudzi mwa Wimbe kwa mfumu yaikulu Wimbe mb’oma la Kasungu.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>