Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Woyimira Anthu pa Milandu Wapezeka Atafa Mdziko la Kenya

$
0
0

Loya wina yemwe amayimilira  munthu wina pamlandu woti apolisi m`dziko la Kenyaakumachitira nkhanza  anthu m`dzikolo wapezeka  atafa munzinda wa Nairobi m`dzikolo.

Loyayu, Willie Kimani wa zaka 32, pamodzi ndi dalaivala yemwe  amamuyendetsa pathawiyo anasowa sabata yapitayo atangotuluka mu  bwalo la milandu. Thupi la mkuluyu ati alipeza litakulungidwa  m`phepete mwa mtsinje wina omwe uli pamtunda  wa makilomita 70 kumwera chakum`mawa kwa  mzinda wa Nairobi.

Bungwe la Malamulo m`dzikolo lati kuphedwa kwa loyayu ndi chinthu chomvetsa chisoni kwambiri pantchito yoteteza malamulo a dzikolo.

Apolisi mdziko la Kenya akhala akudzudzulidwa kuti amachitira nkhanza mzika zadzikolo komanso kugwirizana ndi mbava  polimbikitsa umbanda ndi umbava.

Pakadali pano mkulu wa apolisi mdzikolo walamula kuti apolisi atatu amene akuganiziridwa kuti ndi amene achita izi amangidwe.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>