Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Amuna Awiri Amangidwa Kamba Kobera Mayeso a MSCE

$
0
0

Amuna awiri ali m’manja mwa apolisi atapezeka akubera mayeso a fomu 4 m’boma la Balaka.

M’modzi mwa amunawa a Joseph Makiyi omwe amagwira ntchito ku Prison Fellowship anatenga tchuthi kuntchito kwawo kuti akukalemba mayeso a MSCE ku Balaka Islamic Institute ndipo m’malo mwake anapempha mzawo a Charles Kumwenda omwe amagwira ntchito  ngati wa zaumoyo pa chipatala cha Kapire m’bomalo kuti akawalembere mayesowo.

Masana a tsiku la pa 30 June pamene ophunzira amalemba mayeso a Human Geography ndi pamene mkuluyi anagwidwa ndi m’modzi mwa ogwira ntchito ku MANEB yemwe anafika kudzayang’nira m’mene mayeso amayendera pa malopa.

Pakadali pano amuna awiriwa avomera mlanduwu ndipo akuyembekezeka kukawonekera ku bwalo la milandu ndikukayankha mulandu wobera mayeso.

Amunawa amachokera m’mudzi mwa Lupanga mfumu yaikulu Nsamala m’boma la Balaka.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>