Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ambuye Musikuwa Apempha Asisiteri Akhale Odzipereka pa Utumiki

$
0
0

Episkopi wa dayosizi ya Chikwawa ya mpingo wakatolika Ambuye Peter Musikuwa wapempha asisteri kuti azikhala odzipereka pa utumiki wao.

Ambuye Musikuwa alankhula izi pa mwambo wa malumbiro a ku nthawi zonse a asisteri a chipani cha Divine Providence omwe unachitikira ku parishi ya Fatima mu dayosiziyi.

Iwo ati atumikiwa akuyenera kuzindikira kuti satana atha kubwera pakati pawo ndi kuwalepheretsa utumiki wao.

“Satana amabwera mwanjira zosiyanasiyana natiyesa pa malumbiro athu aja koma ngati tilimbika mchikhulupiliro, tikazindikiranso kuti chiyitanidwe ndi chikondi cha Mulungu tizalimbika mu utumiki wathu komanso chiitanidwe,” anatero Ambuye Musikuwa.

Ambuye Musikuwa anati, “Tikuyeneranso kudziwa kuti Mulungu anatiyitana kuti tikhale zida zake zoti azigwiritse ntchito yopulumutsira anthu. Munthu woyitanidwa ndi chida cha Mulungu. Choncho tikuyenera kukhala okonzeka nthawi zonse kuti Mulungu atigwiritse ntchito. Tikuyenera kukhala ndi mtima ngati wa Simoni woti chifukwa cha mawu anu tisunthira kozamako.”


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>