Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

MWAMUNA WINA ALAMULIDWA KUKHALA KUNDENDE ZAKA 8 ATABA MATUMBA 202 A FETEREZA

$
0
0

Bwalo la milandu la magistrate m'boma la Ntchisi lalamula mwamuna wina wa zaka 27, kuti akakhale kundende zaka zisanu ndi zitatu (8), atapezeka olakwa pa mlandu woba fetereza ndi mbewu za ndalama zoposa MK 4.9 million ku kampani ya Export Trading .

Mneneri wa apolisi m'bomalo Seargent Gladson M’bumpha wati mwamunayo Steven Kalipinde, anaba matumba a feteleza wa Urea okwana 202 komanso wa NPK  ku kampaniyo. Wapolisi otengera  milandu kubwalo la milandu , Constable Austin Daudi, anauza bwalolo kuti a Kalipinde, anabanso mbeu ndi katundu wina zomwe ndi zandalama zoposa 4.9 million kwacha. Popereka chigamulo chake magistrate Dorothy Kalua, anati wapereka chilango chokhwimacho kuti anthu ena atengerepo phunziro. A Steven Kalipinde amachokera m'mudzi wa Chipho kwa mfumu yaikulu Msabwe mboma la Thyolo.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>